15. amenewo, m'mene adatsikirako, anawapempherera, kuti alandire Mzimu Woyera:
16. pakuti kufikira pamenepo nkuti asanagwe pa wina mmodzi wa iwo; koma anangobatizidwam'dzina la Ambuye Yesu.
17. Pamenepo anaika manja pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.
18. Koma pakuona Simoni kuti mwa kuika manja a atumwi anapatsidwa Mzimu Woyera, anawatengera ndalama,
19. nanena, Ndipatseni inenso ulamuliro umene, kuti amene ali yense ndikaika manja pa iye, alandire Mzimu Woyera.