Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 7:47-54 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

47. Kama 19 Solomo anammangira nyumba.

48. Komatu 20 Wamwambamwambayo sakhala m'nyumba zomangidwa ndi manja; monga mneneri anena,

49. 21 Thambo la kumwamba ndilo mpando wacifumu wanga,Ndi dziko lapansi copondapo mapazi anga:Mudzandimangira nyumba yotani? ati Ambuye;Kapena malo a mpumulo wanga ndi otani?

50. Silinapanga dzanja langa zinthu izi zonse kodi?

51. 22 Ouma khosi ndi osadulidwa mtima ndi makutu inu, mukaniza Mzimu Woyera nthawi zonse; monga anacita makolo anu, momwemo inu.

52. 23 ndiye yani wa aneneri makolo anu sanamzunza? ndipo anawapha iwo amene anaonetseratu za kudzakwace kwa Wolungamayo; wa iye amene mwakhala tsopano akumpereka ndi akumupha;

53. inu amene munalandira cilamulo 24 monga cidaikidwa ndi angelo, ndipo simunacisunga.

54. Koma pakumva izi analaswa mtima, namkukutira mano.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 7