Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 7:44-58 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. Cihema ca umboni cinali ndi makolo athu m'cipululu, monga adalamula iye wakulankhula ndi Mose, 16 acipange ici monga mwa cithunzico adaciona.

45. 17 Cimenenso makolo athu akudza m'mbuyo, analowa naco ndi Y oswa polandira iwo zao za amitundu, 18 amene Mulungu anawaingitsa pamaso pa makolo athu, kufikira masiku a Davine;

46. amene anapeza cisomo pamaso pa Mulungu, napempha kuti apeze mokhalama Mulungu wa Yakobo.

47. Kama 19 Solomo anammangira nyumba.

48. Komatu 20 Wamwambamwambayo sakhala m'nyumba zomangidwa ndi manja; monga mneneri anena,

49. 21 Thambo la kumwamba ndilo mpando wacifumu wanga,Ndi dziko lapansi copondapo mapazi anga:Mudzandimangira nyumba yotani? ati Ambuye;Kapena malo a mpumulo wanga ndi otani?

50. Silinapanga dzanja langa zinthu izi zonse kodi?

51. 22 Ouma khosi ndi osadulidwa mtima ndi makutu inu, mukaniza Mzimu Woyera nthawi zonse; monga anacita makolo anu, momwemo inu.

52. 23 ndiye yani wa aneneri makolo anu sanamzunza? ndipo anawapha iwo amene anaonetseratu za kudzakwace kwa Wolungamayo; wa iye amene mwakhala tsopano akumpereka ndi akumupha;

53. inu amene munalandira cilamulo 24 monga cidaikidwa ndi angelo, ndipo simunacisunga.

54. Koma pakumva izi analaswa mtima, namkukutira mano.

55. Koma iye, 25 pokhala wodzala ndi Mzimu Woyera, anapenyetsetsa Kumwamba, naona ulemerero wa Mulungu, ndi Yesu alikuimirira pa dzanja lamanja la Mulungu,

56. nati, Taonani, 26 ndipenya m'Mwamba motseguka, ndi Mwana wa munthu alikuimirira pa dzanja lamanja la Mulungu.

57. Koma anapfuula ndi mau akuru, natseka m'makutu mwao, namgumukira iye ndi mtima umodzi;

58. ndipo 27 anamtaya kunja kwa mudzi, namponya miyala; ndipo 28 mbonizo zinaika zobvala zao pa mapazi a mnyamata dzina lace Saulo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 7