Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 7:40-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. 11 nati ndi Aroni, Tipangireni milungu yotitsogoleraife; pakuti Mose uja, amene anatiturutsa m'Aigupto, sitidziwa comwe camgwera.

41. Ndipo 12 anapanga mwana wa ng'ombe masiku omwewo, nabwera nayo nsembe kwa fanolo, nasekerera ndi nchito za manja ao.

42. Koma 13 Mulungu anatembenuka, nawapereka iwo atumikire gulu la kumwamba; monga kwalembedwa m'buku laaneneri,14 Kodi mwapereka kwa Ine nyama zophedwa ndi nsembeZaka makumi anai m'cipululu, nyumba ya Israyeli inu?

43. 15 Ndipo munatenga cihema ca Moloki,Ndi nyenyezi ya mulungu Refani,Zithunzizo mudazipanga kuzilambira;Ndipo ndidzakutengani kunka nanu m'tsogolo mwace mwa Babulo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 7