Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 7:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Koma pamene zaka zace zinafikira ngati makumi anai, kunalowa mumtima mwace kuzonda abale ace ana a Israyeli,

24. Ndipo pakuona wina woti alikumcitira cotpa, iye anamcinjiriza, nambwezera cilango wozunzayo, nakantha M-aigupto.

25. Ndipo anayesa kuti abale ace akazindikira kuti Mulungu alikuwapatsa cipulumutso mwa dzanja lace; koma sanazindikira.

26. Ndipo m'mawa mwace anawaonekera alikulimbana ndeu, ndipo anati awateteze, ayanjanenso, nati, Amuna inu, muli abale; mucitirana coipa bwanji?

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 7