Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 7:13-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo pa ulendo waciwiri Y osefe anazindikirika ndi abale ace; ndipo pfuko la Yosefe linaonekera kwa Farao.

14. Ndipo Yosefe anatumiza, naitana Yakobo atate wace, ndi a banja lace lonse, ndiwo anthu makumi asanu ndi awiri mphambu asanu.

15. Ndipo Yakobo anatsikira ku Aigupto; ndipo anamwalira, iye ndi makolo athu;

16. ndipo anawanyamula kupita nao ku Sukemu, nawaika m'manda amene Abrahamu adagula ndi mtengo wace wa ndalama kwa ana a Emori m'Sukemu.

17. Koma m'mene inayandikira nthawi ya lonjezo limene Mulungu adalonjezana ndi Abrahamu, anthuwo anakula nacuruka m'Aigupto,

18. kufikira inauka mfumu yina pa Aigupto, imene siinamdziwa Yosefe.

19. Imeneyo inacenjerera pfuko lathu, niwacitira coipa makolo athu, niwatayitsa tiana tao, kuti tingakhale ndi moyo.

20. Nyengo yomweyo anabadwa Mose, ndiye wokoma ndithu; ndipo anamlera miyezi itatu m'nyumba ya atate wace:

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 7