Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 5:9-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Koma Petro anati kwa iye, Munapangana pamodzi bwanji kuyesa Mzimu wa Ambuye? Taona, mapazi ao a iwo amene anaika mwamuna wako ali pakhomo, ndipo adzakunyamula kuturuka nawe.

10. Ndipo anagwa pansi pomwepo pa mapazi ace, namwalira; ndipo analowa anyamatawo, nampeza iye wafa, ndipo anamnyamula kuturuka naye, namuika kwa mwamuna wace.

11. Ndipo anadza mantha akuru pa Mpingo wonse, ndi pa onse akumvaizi.

12. Ndipo mwa manja aatumwi zizindikilo ndi zozizwa zambiri zinacitidwa pa anthu; ndipo anali onse ndi mtima umodzi m'khumbi la Solomo.

13. Koma palibe mmodzi wa otsalawo analimba mtima kuphatikana nao; komatu anthu anawakuzitsa;

14. ndipo makamaka anaonjezedwa kwa Ambuye okhulupirira ambiri, ndiwo amuna ndi akazi;

15. kotero kuti ananyamulanso naturuka nao odwala Ifumakwalala, nawaika pamakama ndi pamphasa, kuti, popita Petro, ngakhale cithunzi cace cigwere wina wa iwo.

16. Komanso unasonkhana pamodzi unyinji wa anthu ocokera ku midzi yozungulira Yerusalemu, alikutenga odwala, ndi obvutika ndi mizimu yonyansa; ndipo anaciritsidwa onsewa.

17. Koma anauka mkulu wa ansembe ndi onse amene anali naye, ndiwo a cipatuko ca Asaduki, nadukidwa,

18. nathira manja atumwi, nawaika m'ndende ya anthu wamba.

19. Koma mngelo wa Ambuye anatsegula pakhomo pa ndende usiku, nawaturutsa, nati,

20. Pitani, ndipo imirirani, nimulankhule m'Kacisi kwa anthu onse mau a Moyo umene.

21. Ndipo atamva ici, analowa m'Kacisi mbanda kuca, naphunzitsa. Koma anadza mkulu wa ansembe ndi iwo amene analinaye, nasonkhanitsa a bwalo la akuru, ndi akulu onse a ana a Israyeli, natuma kundende atengedwe ajawo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 5