Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 5:20-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Pitani, ndipo imirirani, nimulankhule m'Kacisi kwa anthu onse mau a Moyo umene.

21. Ndipo atamva ici, analowa m'Kacisi mbanda kuca, naphunzitsa. Koma anadza mkulu wa ansembe ndi iwo amene analinaye, nasonkhanitsa a bwalo la akuru, ndi akulu onse a ana a Israyeli, natuma kundende atengedwe ajawo.

22. Koma anyamata amene adafikako sanawapeza m'ndende, ndipo pobwera anafotokoza,

23. nanena, Nyumba yandende tinapeza citsekere, ndi alonda alikuimirira pamakomo; koma pamene tinatsegula sitinapezamo mmodzi yense.

24. Koma m'mene anamva mau awa mdindo wa Kacisi ndi ansembe akulu anathedwa nzeru ndi iwo aja, kuti ici cidzatani.

25. Ndipo anadza wina nawafotokozera, kuti, Taonani, amuna aja mudawaika m'ndende ali m'Kacisi, alikuimirira ndi kuphunzitsa anthu.

26. Pamenepo anacoka mdindo pamodzi ndi anyamata; nadza nao, koma osawagwiritsa, pakuti anaopa anthu, angaponyedwe miyala.

27. Ndipo m'mene adadza nao, anawaika pa bwalo la akuru. Ndipo anawafunsa mkuru wa ansembe,

28. nanena, Tidakulamulirani cilamulire, musaphunzitsa kuchula dzina ili; ndipo taonani, mwadzaza Yerusalemu ndi ciphunzitso canu, ndipo mufuna kutidzetsera ife mwazi wa munthu uja.

29. Ndipo anayankha Petro ndi atumwi, nati, Tiyenera kumvera Mulungu koposa anthu.

30. Mulungu wa makolo athu anaukitsa Yesu, amene munamupha inu, ndi kumpacika pamtengo.

31. Ameneyo Mulungu anamkweza ndi dzanja lace lamanja, akhale Mtsogoleri ndi Mpulumutsi, kuti apatse kwa Israyeli kulapa, ndi cikhululukiro ca macimo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 5