Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 5:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. nathira manja atumwi, nawaika m'ndende ya anthu wamba.

19. Koma mngelo wa Ambuye anatsegula pakhomo pa ndende usiku, nawaturutsa, nati,

20. Pitani, ndipo imirirani, nimulankhule m'Kacisi kwa anthu onse mau a Moyo umene.

21. Ndipo atamva ici, analowa m'Kacisi mbanda kuca, naphunzitsa. Koma anadza mkulu wa ansembe ndi iwo amene analinaye, nasonkhanitsa a bwalo la akuru, ndi akulu onse a ana a Israyeli, natuma kundende atengedwe ajawo.

22. Koma anyamata amene adafikako sanawapeza m'ndende, ndipo pobwera anafotokoza,

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 5