Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 4:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. obvutika mtima cifukwa anaphunzitsa anthuwo, nalalikira mwa Yesu kuuka kwa akufa.

3. Ndipo anawathira manja, nawaika m'ndende kufikira m'mawa; pakuti mpa madzulo pamenepo.

4. Koma ambiri a iwo amene adamva mau anakhulupira; ndipo ciwerengero ca amuna cinali ngati zikwi zisanu.

5. Koma panali m'mawa mwace, anasonkhana pamodzi m'Yerusalemu oweruza, ndi akulu, ndi alembi;

6. ndi Anasi mkulu wa ansembe, ndi Kayafa, ndi Yohane, ndi Alesandro, ndi onse amene anali a pfuko la mkulu waansembe.

7. Ndipo m'mene anawaimika pakati, anafunsa kuti, Ndi mphamvu yanji, kapena m'dzina lanji, mwacita ici inu?

8. Pamenepo Petro, wodzala ndi Mzimu Woyera anati kwa iwo, Oweruza a anthu inu, ndi akulu,

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 4