Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 3:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. ameneyo, pakuona Petro ndi Yohane akuti alowe m'Kacisi, anapempha alandire caulere.

4. Ndipo Petro, pompenyetsetsa iye pamodzi ndi Yohane, anati, Tiyang'ane ife.

5. Ndipo iye anabvomereza iwo, nalingirira kuti adzalandira kanthu.

6. Koma Petro anati, Siliva ndi golidi ndiribe; koma cimene ndiri naco, ici ndikupatsa, M'dzina la Yesu Kristu Mnazarayo, yenda,

7. Ndipo anamgwira Iye ku dzanja lace lamanja, namnyamutsa; ndipo pomwepo mapazi ace ndi mfundo za kumapazi zinalimbikitsidwa.

8. Ndipo anazunzuka, naimirira, nayenda; ndipo analowa pamodzi nao m'Kacisi, nayenda, nalumpha, nayamika Mulungu.

9. Ndipo anthu onse anamuona iye, alikuyenda ndi kuyamika Mulungu;

10. namzindikira iye, kuti ndiye amene anakhala pa Khomo Lokongola la Kacisi: ndipo anadzazidwa ndi kudabwa ndi kuzizwa pa ici cidamgwera.

11. Koma m'mene anagwira Petro ndi Yohane, anawathamangira pamodzi anthu onse ku khumbi lochedwa la Solomo, alikudabwa ndithu.

12. Koma m'mene Petro anaciona, anayankha kwa anthu, Amuna inu a Israyeli, muzizwa naye bwanji ameneyo? kapena mutipenyetsetsa ife bwanji, monga ngati tamyendetsa iye ndi mphamvu ya ife eni, kapena ndi cipembedzo cathu?

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 3