Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 3:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma inu munakaniza Woyera ndi Wolungamayo, ndipo munapempha kuti munthu wambanda apatsidwe kwa inu,

15. ndipo munamupha Mkulu wa moyo; amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa; za ici ife tiri mboni.

16. Ndipo pa cikhulupiriro ca m'dzina lace dzina lacelo linalimbikitsa iye amene mumuona, nimumdziwa; ndipo cikhulupiriro ciri mwa iye cinampatsa kucira konse kumeneku pamaso pa inu nonse.

17. Ndipo tsopano, abale, ndidziwa kuti munacicita mosadziwa, monganso akulu anu.

18. Koma zimene Mulungu analalikiratu m'kamwa mwa aneneri onse, kuti adzamva kuwawa Kristu, iye anakwaniritsa cotero.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 3