Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 3:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Mulungu wa Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo, Mulungu wa makolo athu, analemekeza Mwana wace Yesu; amene, inu munampereka ndi kumkaniza pa Pilato, poweruza iyeyu kummasula.

14. Koma inu munakaniza Woyera ndi Wolungamayo, ndipo munapempha kuti munthu wambanda apatsidwe kwa inu,

15. ndipo munamupha Mkulu wa moyo; amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa; za ici ife tiri mboni.

16. Ndipo pa cikhulupiriro ca m'dzina lace dzina lacelo linalimbikitsa iye amene mumuona, nimumdziwa; ndipo cikhulupiriro ciri mwa iye cinampatsa kucira konse kumeneku pamaso pa inu nonse.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 3