Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 3:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma Petro ndi Yohane analikukwera kunka kuKacisi pa ora lakupembedza, ndilo lacisanu ndi cinai.

2. Ndipo munthu wina wopunduka miyendo cibadwire ananyamulidwa, amene akamuika masiku onse pa khomo la Kacisi lochedwa Lokongola, kuti apemphe zaulere kwa iwo akulowa m'Kacisi;

3. ameneyo, pakuona Petro ndi Yohane akuti alowe m'Kacisi, anapempha alandire caulere.

4. Ndipo Petro, pompenyetsetsa iye pamodzi ndi Yohane, anati, Tiyang'ane ife.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 3