Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 28:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo kunatero kuti atate wace wa Popliyo anagona wodwala nthenda ya malungo ndi kamwazi. Kwa iyeyu Paulo analowa, napemphera, naika manja pa iye, namciritsa.

9. Ndipo patacitika ici, enanso a m'cisumbu, okhala nazo nthenda, anadza, naciritsidwa;

10. amenenso anaticitira ulemu wambiri; ndipo pocoka ife anatiikira zotisowa.

11. Ndipo itapita miyezi itatu tinayenda m'ngalawa ya ku Alesandriya, idagonera nyengo ya cisanu kucisumbuko, cizindikilo cace, Ana-a-mapasa.

12. Ndipo pamene tinakoceza ku Surakusa, tinatsotsako masiku atatu.

13. Ndipo pocokapo tinapaza ntifika ku Regio; ndipo litapita tsiku limodzi unayamba mwela, ndipo m'mawa mwace tinafika ku Potiyolo:

14. pamenepo tinakomana ndi abale, amene anatiumirira tikhale nao masiku asanu ndi awiri; ndipo potero tinafika ku Roma.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 28