15. Kucokera kumeneko abalewo, pakumva za ife, anadza kukomana nafe ku Bwalo la Apiyo, ndi ku Nyumba za Alendo Zitatu; ndipo pamene Paulo anawaona, anayamika Mulungu, nalimbika mtima.
16. Ndipo pamene tinalowa m'Roma, analola Paulo akhale pa yekha ndi msilikari womdikira iye.
17. Ndipo kunali, atapita masiku atatu, anaitana akulu a Ayuda asonkhane; ndipo atasonkhana, ananena nao, Ine, amuna, abale, ndingakhale sindinacita kanthu kakuipsa anthu, kapena miyambo ya makolo, anandipereka wam'nsinga kucokera ku Yerusalemu ku manja a Aroma;
18. ndiwo, atandifunsafunsa ine anafuna kundimasula, popeza panalibe cifukwa ca kundiphera.