Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 27:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo Itapita nthawi yambiri, ndipo unayambokhala woopsya ulendowo, popezanso nyengo ya kusala cakudya idapita kale, Paulo anawacenjeza,

10. nanena nao, Amuna inu, ndiona ine kuti ulendo udzatitengera kuonongeka ndi kutayika kwambiri, si kwa akatundu okha kapena ngalawa yokha, komatunso kwa moyo wathu.

11. Koma kenturiyo anakhulupirira watsigiro ndi mwini ngalawa makamaka, wosasamala mau a Paulo.

12. Ndipo popezadooko silinakoma kugonapo nyengo yacisanu, unyinji unacita uphungu ndi kutiamasule nacokepo, ngati kapena nkutheka afikire ku Foinika, ndi kugonako, ndilo dooko la ku Krete, loloza kumpoto ndi kumwela.

13. Ndipo poomba pang'ono mwela, poyesa kuti anaona cofunirako, anakoka nangula, napita m'mbali mwa Krete.

14. Koma patapita pang'ono idaombetsa kucokerako mphepo ya namondwe, yonenedwa Eurokulo;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 27