Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 27:24-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. nanena, Usaope Paulo; ukaimirira pamaso pa Kaisara; ndipo, taona, Mulungu anakupatsa onse amene akuyenda nawe pamodzi.

25. Cifukwa cace, limbikani mtima, amuna inu; pakuti ndikhulupirira Mulungu, kuti kudzatero monga momwe ananena ndi ine.

26. Koma tiyenera kutayika pa cisumbu cakuti.

27. Koma pofika usiku wakhumi ndi cinai, potengedwa ife kwina ndi kwina m'nyanja ya Adriya, pakati pa usiku amarinyero anazindikira kuti analikuyandikira kumtunda;

28. ndipo anayesa madzi, napeza mikwamba makumi awiri; ndipo katapita kanthawi, anayesanso, napeza mikwamba khumi ndi isanu.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 27