Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 27:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo pamene padatsimikizika kuti tipite m'ngalawa kunka ku Italiya, anapereka Paulo ndi andende ena kwa kenturiyo dzina lace Yuliyo, wa gulu la Augusto.

2. Ndipo m'mene tidalowam'ngalawa ya ku Adramutiyo ikati ipite kunka ku malo a ku mbali ya Asiya, dnakankha, ndipo Aristarko Mmakedoniya wa ku Tesalonika, anali nafe.

3. Ndipo m'mawa mwace tinangokoceza ku Sidoni; ndipo Yuliyo anacitira Paulo mwacikondi, namlola apite kwa abwenzi ace amcereze.

4. Ndipo pokankhanso pamenepo, tinapita kutseri kwa Kupro, popeza mphepo inaomba mokomana nafe.

5. Ndipo pamene tidapyola nyanja ya kunsi kwace kwa Kilikiya ndi Pamfiliya, tinafika ku Mura wa Lukiya.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 27