Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 26:28-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndipo Agripa anati kwa Paulo, Ndi kundikopa pang'ono ufuna kundiyesera Mkristu.

29. Ndipo Paulo anati, Mwenzi atalola Mulungu, kuti ndi kukopa pang'ono, kapena ndi kukopa kwambiri, si inu nokha, komatunso onse akundimva ine lero, akadakhala otero onga ndiri ine, osanena nsinga izi.

30. Ndipo ananyamuka mfumu, ndi kazembe, ndi Bemike, ndi iwo akukhala nao;

31. ndipo atapita padera analankhula wina ndi mnzace, nanena, Munthu uyu sanacita kanthu koyenera imfa, kapena nsinga.

32. Ndipo Agripa anati kwa Festo, Tikadakhoza kumasula munthuyu, wakadapanda kunena, Ndikaturukire kwa Kaisara.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 26