22. Pamenepo pothandizidwa ndi Mulungu, ndiimirira kufikira lero lino, ndi kuwacitira umboni ang'ono ndi akuru, posanena kanthu kena koma zimene aneneri ndi Mose ananenazidzafika;
23. kuti Kristu akamve zowawa, kuti iye, woyamba mwa kuuka kwa akufa, adzalalikira kuunika kwa anthu ndi kwa amitundu.
24. Koma pakudzikanira momwemo, Festo anati ndi mau akuru, Uli wamisala Paulo; kuwerengetsa kwako kwakucititsa misala.
25. Koma Paulo anati, Ndiribe misala, Festo womvekatu; koma nditurutsa mau a coonadi ndi odziletsa.
26. Pakuti mfumuyo idziwa izi, kwa iye imene ndilankhula nayonso mosaopa: pakuti ndidziwadi kuti kulibe kanthu ka izi kadambisikira; pakuti ici Sicinacitika m'tseri.