Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 24:3-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. tizilandira ndi ciyamiko conse, monsemo ndi ponsepo, Felike womveka inu.

4. Koma kuti ndingaonjeze kukulemetsani ndikupempha, ni mutimvere mwacidule ndi cifatso canu.

5. Pakuti tapeza munthuyu ali ngati mliri, ndi woutsa mapanduko kwa Ayuda onse m'dziko lonse lokhalamo anthu, ndi mtsogoleri wa mpanduko wa Anazarene;

6. amenenso anayesa kuipsa Kacisi; amene tamgwira;

8. kwa iye mudzakhoza kuzindikira pomfunsa nokha, za izi zonse timnenerazi.

9. Ndipo Ayudanso anabvomerezana naye, natsimikiza kuti izi zitero.

10. Ndipo pamene kazembe anamkodola kuti anene, Paulo anayankha, Podziwa ine kuti mwakhala woweruza wa mtundu uwu zaka zambiri, ndidzikanira mokondwera;

11. popeza mukhoza kuzindikira kuti apita masiku khumi ndi awiri okha cikwerere ine ku Yerusalemu kukalambira;

12. ndipo sanandipeza m'Kacisi wotsutsana ndi munthu, kapena kuutsa khamu la anthu, kapena m'sunagoge kapena m'mzinda.

13. Ndipo sangathe kukutsimikizirani zimene andinenera ine tsopano.

14. Koma ici ndibvomera kwa inu, kuti monga mwa Njira yonenedwa mpatuko, momwemo nditumikira Mulungu wa makolo athu, ndi kukhulupira zonse ziri monga mwa cilamulo, ndi zolembedwa mwa aneneri;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 24