Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 24:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma ici ndibvomera kwa inu, kuti monga mwa Njira yonenedwa mpatuko, momwemo nditumikira Mulungu wa makolo athu, ndi kukhulupira zonse ziri monga mwa cilamulo, ndi zolembedwa mwa aneneri;

15. ndi kukhala naco ciyembekezo ca kwa Mulungu cimene iwo okhanso acilandira, kuti kudzakhala kuuka kwa olungama ndi osalungama.

16. M'menemonso ndidziyesera ndekha ndikhale naco nthawi zonse cikumbu mtima cosanditsutsa ca kwa Mulungu ndi kwa anthu.

17. Ndipo zitapita zaka zambiri ndinadza kutengera mtundu wanga zacifundo, ndi zopereka;

18. popereka izi anandipeza woyeretsedwa m'Kacisi, wopanda khamu la anthu, kapena phokoso; koma panali Ayuda ena a ku Asiya,

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 24