Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 23:31-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Pamenepo ndipo asilikari, monga adawalamulira, anatenga Paulo, napita naye usiku ku Antipatri.

32. Koma m'mawa mwace anasiya apakavalo amperekeze, nabwera kulinga;

33. iwowo, m'mene anafika ku Kaisareya, anapereka kalata kwa kazembe, naperekanso Paulo kwa iye.

34. Ndipo m'mene adawerenga anafunsa acokera m'dziko liti; ndipo pozindikira kuti anali wa ku Kilikiya,

35. anati, Ndidzamva mlandu wako, pamene akukunenera afika. Ndipo analamulira kuti amdikire iye m'nyumba yamlandu ya Herode.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 23