Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 23:26-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Klaudiyo Lusiya kwa kazembe womveketsa Felike, ndikulankhulani.

27. Munthu uyu anagwiridwa ndi Ayuda, ndipo akadaphedwa ndi iwo; pamenepo ndinafikako ine ndi asilikari, ndipo ndinamlanditsa pakumva kuti ndiye Mroma.

28. Ndipo pofuna kuzindikira cifukwa cakuti anamnenera iye, ndinatsikira naye ku bwalo la akuru ao.

29. Ndipo ndinapeza kuti adamnenera za mafunso a cilamulo cao; koma analibe kumnenera kanthu kakuyenera imfa kapena nsinga.

30. Ndipo m'mene anandidziwitsa kuti pali ciwembu ca pa munthuyu, pomwepo ndinamtumiza kwa inu; ndipo ndalamulira akumnenera akamnenere kwa inu.

31. Pamenepo ndipo asilikari, monga adawalamulira, anatenga Paulo, napita naye usiku ku Antipatri.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 23