Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 22:9-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo iwo akukhala nane anaonadi kuunika, koma sanamva mau akulankhula nane.

10. Ndipo ndinati, ndidzacita ciani, Ambuye? Ndipo Ambuye anati kwa ine, Taukavpita ku Damasiko; kumeneko adzakufotokozera zonse zoikika kwa iwe uzicite.

11. Ndipo popeza sindinapenya, cifukwa ca ulemerero wa kuunikako, anandigwira dzanja iwo amene anali ndi ine, ndipo ndinafika ku Damasiko.

12. Ndipo munthu dzina lace Hananiya, ndiye munthu wopembedza monga mwa cilamulo, amene amcitira umboni wabwino Ayuda onse akukhalako,

13. anadza kwa ine, ndipo poimirirapo anati kwa ine, Saulo, mbale, penyanso. Ndipo ine, ora lomweli ndinampenya.

14. Ndipo anati, Mulungu wa makolo athu anakusankhiratu udziwe cifuniro cace, nuone Wolungamayo, numve mau oturuka m'kamwa mwace.

15. Ndipo udzamkhalira iye mboni kwa anthu onse, za izo udaziona ndi kuzimva.

16. Ndipo tsopano ucedweranji? Tauka, nubatizidwe ndi kusamba kucotsa macimo ako, nuitane pa dzina lace.

17. Ndipo kunali, nditabwera ku Yerusalemu ndinalikupemphera m'Kacisi, ndinacita ngati kukomoka,

18. ndipo ndinamuona iye, nanena nane, Fulumira, turuka msanga m'Yerusalemu; popeza sadzalandira umboni wako wakunena za Ine.

19. Ndipo ndinati ine, Ambuye, adziwa iwo okha kuti ndinali kuika m'ndende ndi kuwapanda m'masunagoge onse iwo akukhulupirira Inu;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 22