Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 22:15-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo udzamkhalira iye mboni kwa anthu onse, za izo udaziona ndi kuzimva.

16. Ndipo tsopano ucedweranji? Tauka, nubatizidwe ndi kusamba kucotsa macimo ako, nuitane pa dzina lace.

17. Ndipo kunali, nditabwera ku Yerusalemu ndinalikupemphera m'Kacisi, ndinacita ngati kukomoka,

18. ndipo ndinamuona iye, nanena nane, Fulumira, turuka msanga m'Yerusalemu; popeza sadzalandira umboni wako wakunena za Ine.

19. Ndipo ndinati ine, Ambuye, adziwa iwo okha kuti ndinali kuika m'ndende ndi kuwapanda m'masunagoge onse iwo akukhulupirira Inu;

20. ndipo pamene anakhetsa mwazi wa Stefano mboni yanu, ine ndemwe ndinalikuimirirako, ndi kubvomerezana nao, ndi kusunga Zoobvala za iwo amene anamupha iye.

21. Ndipo anati kwa ine, Pita; cifukwa Ine ndidzakutuma iwe kunka kutali kwa amitundu.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 22