15. Ndipo atapita masiku awa tinakonza akatundu athu, ntikwera ku Yerusalemu.
16. Ndipo anamuka nafenso ena a ophunzira a ku Kaisareya, natenganso wina Mnaso wa ku Kupro, wophunzira wakale, amene adzaticereza.
17. Ndipo pofika ife ku Yerusalemu, abale anatilandira mokondwera.
18. Ndipo m'mawa mwace Paulo analowa nafe kwa Yakobo; ndi akulu onse anali pomwepo.
19. Ndipo atawalankhula iwo, anawafotokozera cimodzi cimodzi zimene Mulungu anacita kwa amitundu mwa utumiki wace.