Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 20:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo munali nyali zambiri m'cipinda ca pamwamba m'mene tinasonkhanamo.

9. Ndipo mnyamata dzina lace Utiko anakhala pazenera, wogwidwa nato tulo tatikuru; ndipo pakukhala cifotokozere Paulo, ndipo pogwidwa nato tulo, anagwa posanja paciwiri, ndipo anamtola wakufa.

10. Ndipo potsikirako Paulo, anamgwera namfungatira, nati, Musacite phokoso, pakuti moyo wace ulipo.

11. Ndipo m'mene adakwera, nanyema mkate, nadya, nakamba nao nthawi, kufikira kuca, anacokapo,

12. Ndipo anadza naye mnyamata ali wamoyo, natonthozedwa kwakukuru.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 20