Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 20:31-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Cifukwa cace dikirani, nimukumbukile kuti zaka zitatu sindinaleka usiku ndi usana kucenjeza yense wa inu ndi misozi.

32. Ndipo tsopano ndikuikizani kwa Mulungu, ndi kwa mau a cisomo cace, cimene ciri ndi mphamvu yakumangirira ndi kupatsa inu colowa mwa onse oyeretsedwa.

33. Sindinasirira siliva, kapena golidi, kapena cobvala ca munthu ali yense.

34. Mudziwa inu nokha kuti manja anga awa anatumikira zosowa zanga, ndi za iwo akukhala ndi ine.

35. M'zinthu zonse ndinakupatsani citsanzo, cakuti pogwiritsa nchito, koteromuyenerakuthandiza ofoka ndi kukumbuka mau a Ambuye Yesu, kuti anati yekha, Kupatsa kutidalitsa koposa kulandira.

36. Ndipo m'mene ananena izi, anagwada pansi, napemphera ndi iwo onse.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 20