Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 20:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Koma ife tinatsogolera kunka kungalawa, ndipo tinapita ku Aso, pamenepo tinati timlandire Paulo; pakuti anatipangira comweco, koma anati ayenda pamtunda yekha.

14. Ndipo pamene anakomana ndi ife ku Aso, tinamlandira, ndipo tinafika ku Mitilene.

15. Ndipo m'mene tidacokerapo, m'mawa mwace tinafika pandunjipa Kiyo; ndi m'mawa mwace tinangokoceza ku Samo, ndi m'mawa mwace tinafika ku Mileto.

16. Pakuti Paulo adatsimikiza mtima apitirire pa Efeso, angataye nthawi m'Asiya; pakuti anafulumira, ngati kutheka, akhale ku Yerusalemu tsiku la Pentekoste.

17. Ndipo pokhala ku Mileto anatuma ku Efeso, naitana akulu a Mpingo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 20