Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 2:6-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Koma pocitika mau awa, unyinji wa anthu unasonkhana, nusokonezedwa, popeza yense anawamva alikulankhula m'cilankhulidwe cace ca iye yekha.

7. Ndipo anadabwa onse, nazizwa, nanena, Taonani, awa onse alankhulawa sali Agalileya kodi?

8. ndipo nanga ife timva bwanji, yense m'cilankhulidwe cathu cimene tinabadwa naco?

9. Aparti ndi Amedi, ndi Aelami, ndi iwo akukhala m'Mesopotamiya, m'Yudeya, ndiponso m'Kapadokiya, m'Ponto, ndi m'Asiya;

10. m'Frugiya, ndiponso m'Pamfuliya, m'Aigupto, ndi mbali za Libiya wa ku Kurene, ndi alendo ocokera ku Roma, ndiwo Ayuda, ndiponso opinduka,

11. Akrete, ndi Aarabu, tiwamva iwo alikulankhula m'malilime athu zazikuru za Mulungu.

12. Ndipo anadabwa onse, nathedwa nzeru, nanena wina ndi mnzace, Kodi ici nciani?

13. koma ena anawaseka, nanena kuti, Akhuta vinyo walero.

14. Koma Petro, anaimirira pamodzi ndi khumi ndi mmodziwo, nakweza mau ace, nanena kwa iwo, nati, Amuna inu Ayuda, ndi inu nonse akukhala kwanu m'Yerusalemu, ici cizindikirike kwa inu, ndi po cherani khutu mau anga.

15. Pakuti awa sanaledzera monga muyesa inu; pakuti ndi ora lacitatulokha la tsiku;

16. komatu ici ndi cimene cinanenedwa ndi mneneri Yoeli,

17. Ndipo kudzali m'masiku otsiriza, anena Mulungu,Ndidzathira ca Mzimu wansa pa thupi liri lonse,Ndipo ana anu amuna, ndi akazi adzanenera,Ndipo anyamata anu adzaona masomphenya,Ndi akulu anu adzalota maloto;

18. Ndiponso pa akapolo anga ndi pa adzakazi anga m'masiku awaNdidzathira ca Mzimu wanga; ndipo adzanenera.

19. Ndipo ndidzapatsa zodabwitsa m'thambo la kumwamba,Ndi zizindikilo pa dziko lapansi;Mwazi, ndi moto, ndi mpweya wautsi;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 2