Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 2:42-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Ndipo 4 anali cikhalire m'ciphunzitso ca atumwi ndi m'ciyanjano, m'kunyema mkate ndi mapemphero.

43. Koma panadza mantha pa anthu onse; ndipo 5 zozizwa ndi zizindikilo zambiri zinacitika ndi atumwi.

44. Ndipo onse akukhulupira anali pamodzi, 6 nakhala nazo zonse zodyerana.

45. Ndipo zimene anali nazo, ndi cuma cao, anazigulitsa, nazigawira kwa onse, monga momwe yense anasowera.

46. Ndipo tsiku ndi tsiku 7 anali cikhalire ndi mtima umodzi m'Kacisi, ndipo ananyema mkate kunyumba kwao, nalandira cakudya ndi msangalalo, ndi mtima woona;

47. nalemekeza Mulungu, 8 ndi kukhala naco cisomo ndi anthu onse. Ndipo 9 Ambuye anawaonjezera tsiku ndi tsiku amene akuti apulumutsidwe.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 2