Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 2:30-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Potero, pokhala mneneri iye, ndi kudziwa kuti ndi Iumbiro anamlumbirira Mulungu, kuti mwa cipatso ca m'cuuno mwace adzakhazika wina pa mpando wacifumu wace;

31. iye pakuona ici kale, analankhula za kuuka kwa Kristu, kuti sanasiyidwa m'Hade, ndipo thupi lace silinaona cibvunde.

32. Yesu ameneyo, Mulungu anamuukitsa; za ici tiri mboni ife tonse.

33. Potero, popeza anakwezedwa ndi dzanja Lamanja la Mulungu, nalandira kwa Atate lonjezano la Mzimu Woyera, anatsanulira ici, cimene inu mupenya nimumva.

34. Pakuti Davine sanakwera Kumwamba ai; koma anena yekha,Ambuye anati kwa Mbuye wanga,Khalani ku dzanja lamanja langa,

35. Kufikira ndikaike adani ako copondapo mapazi ako.

36. Pamenepo lizindikiritse ndithu banja liri lonse la Israyeli, kuti Mulungu anamuyesa Ambuye ndi Kristu, Yesu amene inu munampacika.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 2