Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 2:27-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Pakuti simudzasiya moyo wanga ku Hade,Kapena simudzapereka Woyera wanu aone cibvunde,

28. Munandidziwitsa ine njira za moyo;Mudzandidzaza ndi kukondwera pamaso panu.

29. Amuna inu, abale, kuloleka kunena poyera posaopa kwa inu za kholo lija Davine, kuti adamwalira naikidwanso, ndipo manda ace ali ndi ife kufikira lero lino.

30. Potero, pokhala mneneri iye, ndi kudziwa kuti ndi Iumbiro anamlumbirira Mulungu, kuti mwa cipatso ca m'cuuno mwace adzakhazika wina pa mpando wacifumu wace;

31. iye pakuona ici kale, analankhula za kuuka kwa Kristu, kuti sanasiyidwa m'Hade, ndipo thupi lace silinaona cibvunde.

32. Yesu ameneyo, Mulungu anamuukitsa; za ici tiri mboni ife tonse.

33. Potero, popeza anakwezedwa ndi dzanja Lamanja la Mulungu, nalandira kwa Atate lonjezano la Mzimu Woyera, anatsanulira ici, cimene inu mupenya nimumva.

34. Pakuti Davine sanakwera Kumwamba ai; koma anena yekha,Ambuye anati kwa Mbuye wanga,Khalani ku dzanja lamanja langa,

35. Kufikira ndikaike adani ako copondapo mapazi ako.

36. Pamenepo lizindikiritse ndithu banja liri lonse la Israyeli, kuti Mulungu anamuyesa Ambuye ndi Kristu, Yesu amene inu munampacika.

37. Koma pamene anamva ici, analaswa mtima, natitu kwa Petro ndi atumwi enawo, Tidzacita ciani, amuna inu, abale?

38. Koma Petro anati kwa iwo, Lapani, batizidwani yense wa inu m'dzina la Yesu Kristu kuloza ku cikhululukiro ca macimo anu; ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 2