Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 2:23-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. ameneyo, woperekedwa ndi uphungu woikidwa ndi kudziwiratu kwa Mulungu, inu mwampacika ndi kumupha ndi manja a anthu osayeruzika;

24. yemweyo Mulungu anamuukitsa, atamasula zowawa za imfa, mwakuti sikunali kotheka kuti iye agwidwe nayo.

25. Pakuti Davine anena za Iye,Ndinaona Mbuye pamaso panga nthawi zonse;Cifukwa ali pa dzanja langa lamanja, kuti ndingasinthike;

26. Mwa ici unakondwera mtima wanga, ndipo linasangalala lilime langa;Ndipo thupi langanso lidzakhala m'ciyembekezo.

27. Pakuti simudzasiya moyo wanga ku Hade,Kapena simudzapereka Woyera wanu aone cibvunde,

28. Munandidziwitsa ine njira za moyo;Mudzandidzaza ndi kukondwera pamaso panu.

29. Amuna inu, abale, kuloleka kunena poyera posaopa kwa inu za kholo lija Davine, kuti adamwalira naikidwanso, ndipo manda ace ali ndi ife kufikira lero lino.

30. Potero, pokhala mneneri iye, ndi kudziwa kuti ndi Iumbiro anamlumbirira Mulungu, kuti mwa cipatso ca m'cuuno mwace adzakhazika wina pa mpando wacifumu wace;

31. iye pakuona ici kale, analankhula za kuuka kwa Kristu, kuti sanasiyidwa m'Hade, ndipo thupi lace silinaona cibvunde.

32. Yesu ameneyo, Mulungu anamuukitsa; za ici tiri mboni ife tonse.

33. Potero, popeza anakwezedwa ndi dzanja Lamanja la Mulungu, nalandira kwa Atate lonjezano la Mzimu Woyera, anatsanulira ici, cimene inu mupenya nimumva.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 2