37. Pakuti mwatenga anthu awa, osakhala olanda za m'kacisi, kapena ocitira mulungu wathu mwano.
38. Ngati tsono Demetriyo ndi amisiri okhala naye, ali ndi mlandu ndi munthu, mabwalo a mirandu alipo, ndi ziwanga ziripo; anenezane.
39. Koma ngati mufuna kanthu ka zinthu zina, kadzakonzeka m'msonkhano wolamulidwa.
40. Pakutinso palipo potiopsya kuti adzatineneza za cipolowe ca lero; popeza palibe cifukwa ca kufotokozera za cipiringu cimene.
41. Ndipo pamene ananena izi, anamasula msonkhano.