Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 15:32-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Ndipo Yuda ndi Sila, okhala eni okha aneneri, anasangalatsa abale ndi mau ambiri, nawalimbikitsa.

33. Pamene anakhala nthawi, abale analawirana nao ndi mtendere amuke kwa iwo amene anawatumiza. [

34. ]

35. Koma Paulo ndi Bamaba anakhalabe m'Antiokeya, nalinkuphunzitsa, ndi kulalikira mau a Ambuye pamodzi ndi ena ambiri.

36. Patapita masiku, Paulo anati kwa Bamaba, Tibwerenso, tizonde abale m'midzi yonse m'mene tinalalikiramo mau a Ambuye, tione mkhalidwe wao.

37. Ndipo Bamaba anafuna kumtenga Yohane uja, wochedwa Marko.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 15