Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 15:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Tatumiza tsono Yuda ndi Sila, omwenso adzakuuzani ndi mau zinthu zomwezo.

28. Pakuti cinakomer a Mzimu Woyera ndi ife, kuti tisasenzetse inu cothodwetsa cacikuru cina coposa izi zoyenerazi;

29. kuti musale nsembe za mafano, ndi mwazi, ndi zopotola, ndi dama; ngati mudzisungitsa pa zimenezi, kudzakhala bwino kwa inu. Tsalani bwino.

30. Tsono pamene iwo anamuka anatsikira ku Antiokeya; ndipo anasonkhanitsa khamu, napereka kalatayo.

31. Pamene anawerenga, anakondwera cifukwa ca cisangalatso cace.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 15