Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 15:17-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Kuti anthu otsalira afunefune Ambuye,Ndi amitundu onse amene dzina langa linachulidwa pa iwo,

18. Ati Ambuye, amene azidziwitsa zinthu zonsezo ciyambire dzikolapansi.

19. Cifukwa cace ine ndiweruza, kuti tisabvute a mwa amitundu amene anatembenukira kwa Mulungu,

20. koma kuti tilembere kwa iwo, kuti asale zonyansa za mafano, ndi dama, ndi zopotola, ndi mwazi.

21. Pakuti Mose, kuyambira pa mibadwo yakale ali nao m'midzi yonse amene amlalikira, akuwerenga mau ace m'masunagoge masabata onse.

22. Pamenepo cinakomera atumwi ndi akuru ndi Eklesia yensekusankha anthu a m'gulu lao, ndi kuwatumiza ku Antiokeya ndi Paulo ndi Bamaba; ndiwo Yuda wochedwa Barsaba, ndi Sila, akuru a mwa abale; ndipo analembera mau natumiza ndi iwo:

23. Atumwi ndi abale akuru kwa abale a mwa amitundu a m'Antiokeya, ndi Suriya, ndi Kilikiya, tikulankhulani:

24. Popeza tamva kuti ena amene anaturuka mwa ife anakubvutani ndi mau, nasoceretsa mitima yanu; amenewo sitinawalamulira;

25. cinatikomera ndi mtima umodzi, tisankhe anthu, ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi okondedwa anthu Bamaba ndi Paulo,

26. anthu amene anapereka moyo wao cifukwa ca dzina la Yesu Kristu Ambuye wathu.

27. Tatumiza tsono Yuda ndi Sila, omwenso adzakuuzani ndi mau zinthu zomwezo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 15