Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 15:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo mau a aneneri abvomereza pamenepo; monga kunalembedwa,

16. Zikatha izo ndidzabwera, Ndidzamanganso cihema ca Davine, cimene cinagwa;Ndidzamanganso zopasuka zace,Ndipo ndidzaciimikanso:

17. Kuti anthu otsalira afunefune Ambuye,Ndi amitundu onse amene dzina langa linachulidwa pa iwo,

18. Ati Ambuye, amene azidziwitsa zinthu zonsezo ciyambire dzikolapansi.

19. Cifukwa cace ine ndiweruza, kuti tisabvute a mwa amitundu amene anatembenukira kwa Mulungu,

20. koma kuti tilembere kwa iwo, kuti asale zonyansa za mafano, ndi dama, ndi zopotola, ndi mwazi.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 15