Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 15:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pamene iwo anatonthola Yakobo anayankha, nati,Abale, mverani ine:

14. Sumeoni wabwereza kuti poyamba Mulungu anayang'anira amitundu, kuti atenge mwa iwo anthu a dzina lace.

15. Ndipo mau a aneneri abvomereza pamenepo; monga kunalembedwa,

16. Zikatha izo ndidzabwera, Ndidzamanganso cihema ca Davine, cimene cinagwa;Ndidzamanganso zopasuka zace,Ndipo ndidzaciimikanso:

17. Kuti anthu otsalira afunefune Ambuye,Ndi amitundu onse amene dzina langa linachulidwa pa iwo,

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 15