Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 13:35-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Cifukwa anenanso m'Salmo lina, 4 Simudzapereka Woyera wanu aone cibvundi.

36. Pakutitu, Davine, m'mene adautumikira uphungu wa Mulungu m'mbadwo mwace mwa iye yekha, anagona tulo, naikidwa kwa makolo ace, naona cibvundi;

37. koma iye amene Mulungu anamuukitsa sanaona cibvundi.

38. Potero padziwike ndi inu amuna abale, 5 kuti mwa iye cilalikidwa kwa inu cikhululukiro ca macimo;

39. ndipo 6 mwa iye yense wokhulupira ayesedwa wolungama kumcotsera zonse zimene simunangathe kudzicotsera poyesedwa wolungama ndi cilamulo ca Mose.

40. Cifukwa cace penyerani, kuti cingadzere inu conenedwa ndi anenenwo:

41. 7 Taona ni, opeputsa inu, zizwani, kanganukani;Kuti ndigwiritsa nchito Ine masikuanu,Nchito imene simudzaikhulupira wina akakuuzani.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 13