Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 13:24-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Yohane atalalikiratu, asanafike iye, ubatizo wa kulapa kwa anthu onse a Israyeli.

25. Ndipo pakukwaniritsa njira yace Yohane, ananena, Muyesa kuti ine ndine yani? Ine sindine iye. Koma taonani, akudza wina wonditsata ine, amene sindiyenera kummasulira nsapato za pa mapazi ace.

26. Amuna, abale, ana a mbadwa ya Abrahamu, ndi iwo mwa inu akuopa Mulungu, kwa ife atumidwa mau a cipulumutso ici.

27. Pakuti iwo akukhala m'Yerusalemu, ndi akulu ao, popeza sanamzindikira iye, ngakhale mau a aneneri owerengedwa masabata onse, anawakwaniritsa pakumtsutsa.

28. Ndipo ngakhale sanapeza cifukwa ca kumphera, anapempha Pilato kuti aphedwe.

29. Ndipo atatsiriza zonse zolembedwa za iye, anamtsitsa kumtengo, namuika m'manda.

30. Koma Mulungu anamuukitsa iye kwa akufa;

31. ndipo 1 anaonekera masiku ambiri ndi iwo amene anamperekeza iye pokwera ku Yerusalemu kucokera ku Galileya, amenewo ndiwo akumcitira umboni tsopano kwa anthu.

32. Ndipo ife tikulalikirani inu Uthenga Wabwino wa 2 lonjezano locitidwa kwa makolo;

33. kuti Mulungu analikwaniritsa ili kwa ana athu pakuukitsa Yesu; monganso mulembedwa m'Salmo laciwiri, Iwe ndiwe Mwana wanga, lero ndakubala.

34. Ndipo kuti anamuukitsa iye kwa akufa, wosabweranso kueibvundi, anateropo, 3 Ndidzakupatsani inu madalitso oyera ndi okhulupirika a Davine.

35. Cifukwa anenanso m'Salmo lina, 4 Simudzapereka Woyera wanu aone cibvundi.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 13