Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 13:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. nati, Wodzala ndi cinyengo conse ndi cenjerero lonse, iwe, mwana wa mdierekezi, mdani wa cilungamo conse, kodi sudzaleka kuipsa njira zolunjika za Ambuye?

11. Ndipo tsopano, taona, dzanja la Ambuye liri pa iwe, ndipo udzakhala wakhungu wosapeoya dzuwa nthawi, Ndipo pomwepo lidamgwera khungu ndi mdima; ndipo anamukamoka oaf una wina womgwira dzanja.

12. Pamenepo kazembe, pakuona cocitikacoanakhulupira, nadabwa naco ciphunzitso ca Ambuye.

13. Ndipo atamasula kucokera ku Pafo a ulendo wace wa Paulo anadza ku Perge wa ku Pamfuliya; koma Yohane anapatukana nao nabwerera kunka ku Yerusalemu.

14. Koma iwowa, atapita pocokera ku Perge anafika ku Antiokeya wa m'Pisidiya; ndipo analowa m'sunagoge tsiku la Sabata, nakhala pansi.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 13