22. Ndipo anthu osonkhanidwawo anapfuula, Ndiwo mau a Mulungu, si a munthu ai.
23. Ndipo pomwepo mngelo wa Ambuye anamkantha, cifukwa sanampatsa Mulungu ulemerero; ndipo anadyedwa ndi mphutsi, natsirizika.
24. Koma mau a Mulungu anakula, nacurukitsa.
25. Ndipo Bamaba ndi Saulo anabwera kucokera ku Yerusalemu m'mene adatsiriza utumiki wao, natenga Yohane wonenedwanso Marko amuke nao.