Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 10:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo m'mene atacoka mngelo amene adalankhula naye, anaitana anyamata ace awiri, ndi msilikari wopembedza, wa iwo amene amtumikira kosaleka;

8. ndipo m'mene adawafotokozerazonse, anawatuma ku Yopa.

9. Koma m'mawa mwace, pokhala paulendo pao iwowa, m'mene anayandikira mudzi, Petro anakwera pachindwi kukapemphera, ngati pa ora lacisanu ndi cimodzi; ndipo anagwidwa njala, nafuna kudya;

10. koma m'mene analikumkonzera cakudya kudamgwera ngati kukomoka;

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 10