38. za Yesu wa ku Nazarete, kuti Mulungu anamdzoza iye ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu; amene anapitapita nacita zabwino, naciritsa onse osautsidwa ndi mdierekezi, pakuti Mulungu anali pamodzi ndi iye.
39. Ndipo ife ndife mboni zazonse adazicita m'dzikola Ayuda ndim'Yerusalemu; amenenso anamupha, nampacika pamtengo,
40. Ameneyo, Mulungu anamuukitsa tsiku lacitatu, nalola kuti aonetsedwe,
41. si kwa anthu onse ai, koma kwa mboni zosankhidwiratu ndi Mulungu, 1 ndiwo ife amene tinadya ndi kumwa naye pamodzi, atauka iye kwa akufa.
42. Ndipo 2 anatilamulira ife tilalikire kwa anthu, ndipo ticite umboni kuti 3 Uyu ndiye amene aikidwa ndi Mulungu akhale woweruza amoyo ndi akufa.
43. 4 Ameneyu aneneri onse amcitira umboni, kuti onse akumkhulupirira iye adzalandira cikhululukiro ca macimo ao, mwa dzina lace.
44. Petro ali cilankhulire, 5 Mzimu Woyera anagwa pa onse akumva mauwo.
45. Ndipo 6 anadabwa okhulupirirawo akumdulidwe onse amene anadza ndi Petro, cifukwa pa 7 amitundunso panathiridwa mphatso ya Mzimu Woyera.
46. Pakuti anawamva iwo alikulankhula ndi malilime, ndi kumkuza Mulungu. Pamenepo Petro anayankha,