Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 1:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Potero kuyenera kuti wina wa amunawo anatsatana nafe nthawi yonseyi Ambuye Yesu analowa naturuka mwa ife,

22. kuyambira ubatizo wa Yohane, kufikira tsiku lija anatengedwa kunka Kumwamba kutisiya ife, mmodzi wa awa akhale mboni ya kuuka kwace pamodzi ndi ife.

23. Ndipo anaimikapo awiri, Yosefe wochedwa Barsaba, amene anachedwanso Yusto, ndi Matiya.

24. Ndipo anapemphera, nati, Inu, Ambuye, wozindikiramitima ya onse, sonyezani mwa awa awiri mmodziyo amene munamsankha,

25. alowe malo a utumiki uwu ndi utumwi, kucokera komwe Yudase anapatukira, kuti apite ku malo a iye yekha.

26. Ndipo anayesa maere pa iwo; ndipo anagwera Matiya; ndipo anawerengedwa pamodzi ndi khumi ndi mmodziwo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 1