Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 8:51-56 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

51. Ndipo pakufika iye kunyumbako, sanaloleza wina kulowa naye pamodzi, koma Petro, ndi Yohane, ndi Yakobo, ndi atate wa mwanayo, ndi amace.

52. Ndipo anthu onse analikumlira iye ndi kudzigugudapacifuwa. Koma iye anati, Musalire; pakuti iye sanafa, koma agona tulo.

53. Ndipo anamseka iye pwepwete podziwa kuti anafa.

54. Ndipo iye anamgwira dzanja lace, naitana, nati, Buthu, tauka.

55. Ndipo mzimu wace unabwera, ndipo anauka pomwepo; ndipo iye anawauza kuti ampatse kanthu ka kudya.

56. Ndipo atate wace ndi amace anadabwa; ndipo analamulira iwo asauze munthu ali yense cimene cinacitika.

Werengani mutu wathunthu Luka 8